PEMPHERO LA MOTO (#13479)

Pemphero lowululidwa ndi Bahá’u’lláh lotchedwa “QadIhtaraqa ‘I-Mukhlisun”  
 Mdzina la Chauta, Mkhala kale, Wamkulukulu  Ndithudi mitima ya okoma mtima yamezedwa ndi moto wampatuko: Lilikuti dangaliro lakuwala kwa maonekedwe Anu? O Okondedwa a mayiko?  
Iwo okhala chifupi Nanu afulatiridwa Mu mdima wandiwe yani: Nanga kuli kuti kuwala kwa mbandakucha wa kugwirizananso ndi Inu? O Khumbo la mayiko. Matupi ya osankhidwa Anu ali chigonere wozizidwa pa mchenga wakutali Ili kuti nyanja ya kupezeka Kwanu, O Inu Odabwitsa wa mayiko? 
 Manja yofunafuna yakwezedwa kumwamba kwa Chisomo Chanu ndi kuwolowa manja. Ili kuti mvula yakupatsa Kwanu, O Woyankha a mayiko? 
Osakhulupirira akwezeka nkhanza mbali zonse mmanja mwawo: Ili kuti mphamvu yakukaniza ya Cholembera Cha chilamulocho, O Ngwazi ya mayiko?  
Kubwentha kwa agalu kwakula mbali zonse: Uli kuti mkango wamnkhalango ya ukulu Wanu, O Namkungwi wa mayiko? Chisanu chakutira anthu onse: Chili kuti chifundizi cha chikondi Chanu, O Moto wa mayiko?  
Masautso afika pa msinkhu wake: Zili kuti zizindikiro za chitsogozo Chanu, O Chipulumutso cha mayiko? Mdima wakutira anthu ambiri: Kuli kuti kunyezimira kwa Ukulu Wanu, O Dangaliro la mayiko?  
Makosi ya wanthu yasololokera ku umbanda: Nanga yali kuti malupanga yakulipsira Kwanu, O Wowononga wa mayiko? Kutsika kwafikapo pa mathero: Chili kuti chipilala cha chikumbutso cha Ulemelero Wanu, O Ulemerero wa mayiko?  
Masautso amukuta Mvumbulutsi wa Dzina Lanu, wa Chifundo Chonse: Chili kuti chisangalalo cha kasupe wa tsiku la Chivumbulutso Chanu, O Chimwemwe cha mayiko? Mabvuto akulu awagwera anthu apadziko: Nanga chilikuti chizindikiro cha chimwemwe Chanu, O Chisangalaro cha mayiko?  
Taonani malo a mbandakucha wa zizindikiro Zanu yamvekedwa ndi maganizo onyansa: Zili kuti zala za ukulu Wanu, O mphamvu za mayiko? Ludzu lagwira anthu anu onse: Uli kuti Mtsinje wa kuolawa manja Kwanu, O Chifundo cha mayiko?  
Umbombo wagwira ukapolo anthu a padziko: Nanga kupatsa kwa umataya kuli kuti, O Ambuye wa mayiko? Taonani uyu wolakwiridwayo yekhayekha kuchilendo: Ali kuti ochereza akumwamba Kwa Chilamulo Chanu, O Wamkulu wa mayiko  
Ndafulatiridwa ku dziko lachilendo: Chili kuti chizindikiro cha kukhulupirira Kwanu, O Wokhulupirira wa mayiko? Mpweteko wa imfa wayalidwa pa anthu onse: Nanga nyanja Yanu youluma yamoyo osatha ili kuti, O Moyo wa mayiko?  
Kunong'ona kwa satana kwa nong'oneza cholengedwa chiri chonse: Nyenyezi zakugwa za moto wanu zili kuti, O Kuwala kwa mayiko? Uchidakwa wa udani wasintha mtundu wa anthu ambiri Ali kuti masiku a ungwiro, O Khumbo la mayiko?  
Taonani Olakwiridwayo wamvekedwa ndi mazunzo pakati pa ma Siriya: Lili kuti Dangaliro la kuwala kwa mbandakucha Wanu, O Kuwala kwa mayiko? Taonani Ndaletsedwa kuyankhula: Tsono ndikuti kudzachokera kasupe wa nthetemya Zanu, O Mbalame ya mayiko?  
Anthu ambiri akutidwa mu zikhulupiriro ndi maganizo osathandiza: Nanga zili kuti mboni za chitsimikizo Chanu, O Wotsimikiza wa mayiko? Bahá alinkutitimira m'nyanja ya msautso: Chili kuti Chombo cha chiombolo Chanu, O Mpulumutsi wa mayiko? Taonani Tsiku la Kasupe wa mawu Anu mu mdima wa chilengedwe: Dzuwa lamlengalenga wa chisomo Chanu lili kuti? O Woninkha Kuwala mayiko?  
Nyali za chowonadi ndi chiyero, zakumvera ndi ulemu zazimitsidwa: Nanga zizindikiro za mkwiyo obwezera zili kuti, O Choyenda cha mayiko?Kodi simudamuoneko amene wapambana mwa Inu Mwini kapena amene asinkhasinkha pa zomwe zamugwera Iye mu njira ya Chikondi Chanu?  
Tsopano cholembera changa chaima, O Wokondedwa wa mayiko. Nthambi za Uzimu za mtengo wa Lote, zakhadzuka kamba ka mphepo ya mkuntho ya chikonzero: Nanga zisalu zakutchinga Kwanu zili kuti, O Ngwazi ya mayiko?  
Nkhopeyi yaphimbika mu dothi la mabodza: Uli kuti mweya wa chisoni Chanu, O Chifundo cha mayiko? Chovala chonyezima chadetsedwa ndi anthu a mabodza: Nanga chiyerocho chili kuti, O Okongoletsa mayiko?  
Nyanja ya chisomo yadetsedwa ndi zomwe manja ya anthu yadzetsa: Ali kuti mafunde a mphatso Yanu, O Khumbo la mayiko? Khomo lotengera ku Malo a Uzimu lakhomedwa kudzera mmantha ya mazunzo Yanu: Uli kuti mpiringidzo wa kuwolowa manja Kwanu, O wotsegula wa mayiko?  
Masamba yachita chikasu ndi mphepo zowononga ya poizoni: Ili kuti mitambo ya mvula yakuwolowa manja kwanu, O Wopatsa wa mayiko? Chilengedwe chadetsedwa ndi donthi la chifwirimbiti cha machimo: Uli kuti mweya wa kukhululukira Kwanu, O Wokhululukira wa mayiko?  
Taonani mnyamatayu ali yekha m’chipululu: Ili kuti mvula ya chisomo cha kumwamba Kwanu, O Wopatsa wa mayiko? O Cholembela Chopatulika, Tamva kuitana konzuna mu dziko la ulemelero: Perekani khutu ku chimene Lilime lalikulu linena, O Wolakwiridwa wa mayiko!  
Sichifukwa cha kuzizira, Kutentha kwa mawu anu kudakawululidwa, O Wofotokoza mwatchutchu wa mayiko? Sichifukwa cha mabvuto, Dzuwa la kudekha Kwanu lidakawala bwanji, O Wowala wa mayiko? Usalire chifukwa cha ochimwa. Iwe unalengedwa kuti ulimbe ndi kukumana nazo, O Wodekha wa mayiko? 
Kuzuna kwake m’kotani kwa mzere wa mbandakucha wa Pangano pakati pa anthu osokoneza, ndi chofuna Chanu kwa Mulungu, O Wokonda wa mayiko. Chifukwa cha Inu chinsalu cha mtendere chaikidwa pa mwamba pa mapiri, ndipo nyanja ya chaulere ikuyendayenda, O Wong’anima wa mayiko? 
Ndi kukhala Kwanu Dzuwa la Umodzi wanu lawala, ndi kuthamangitsidwa Kwanu dziko la Umodzi lapezeka. Khalani odekha, O Inu othamangitsidwa wa mayiko. Tapanga kutsitsidwa kukhala chobvala cha ulemelero, ndipo mabvuto chokongoletsera cha chihema Chanu, O Chonyaditsa cha mayiko.  
Taonani mitima yadzala ndi udani, ndipo kusalabadira ndi Kwanu. O Inu wofufuta machimo wa mayiko. Pamene malupanga adza, pitani patsogolo! Pamene misikiro iwuluka, musaleke! O Inu wodzipereka wa mayiko? 
Kodi simulira, kapena ndidzalire? Kapena ndilire chifukwa cha kuchepa kwa ngwazi Zanu. O Inu Amene mwapangitsa dziko kulira. Indetu, Ndamva kuitana Kwanu, O Wokondedwa wa Ulemerero Wonse; ndipo tsopano khope ya Bahá iwala ndi chifundizi cha mabvuto ndi moto wa kuwala kwa mawu Anu, ndipo Iye wayimirira mu chikhulupiliro pa malo a kudzipereka, kuyang’ana pa Khumbo Lanu. O Wopereka wa mayiko.  
O 'Alí-Akbar, Pereka matamando kwa Ambuye wako chifukwa cha Pempheroli kuti upumeko kunukhira kwa mawu Anga, ndipo ziwani chimene chatisautsa Ife njira ya Mulungu, wokondeka wa mayiko onse. Ndipo ngati onse atumiki awerenga ndi kulingalira ichi, mudzayatsidwa mitsempha yawo moto umene udzayatsa lawi kudziko lonse.

-Bahá'u'lláh
-----------------------

